3 Yohane 1:6-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. amene anacita umboni za cikondi cako pamaso pa Mpingo; ngati uwaperekeza amenewo pa ulendo wao koyenera Mulungu, udzacita bwino:

7. pakuti cifukwa ca dzinali anaturuka, osalandira kanthu kwa amitundu.

8. Cifukwa cace ife tiyenera kulandira otere, kuti tikakhale othandizana naco coonadi,

9. Ndalemba kanthu kwa Mpingo; komatu Diotrefe uja, wofuna kukhala wamkuru wa iwo, satilandira ife.

10. Momwemo, ndikadza ine, ndidzakumbutsa nchito zace zimene aeitazi, zakunena zopanda pace pa ife ndi mau oipa; ndipopopeza izi sizimkwanira, salandira abale iye yekha, ndipo ofuna kuwalandira awaletsa, nawataya kunja powaturutsa mu Mpingo,

3 Yohane 1