3 Yohane 1:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndiribe cimwemwe coposa ici, cakuti ndimva za ana anga kuti alikuyenda m'coonadi.

5. Wokondedwa, ucita cokhulupirika naco ciri conse, uwacitira abale ndi alendo omwe;

6. amene anacita umboni za cikondi cako pamaso pa Mpingo; ngati uwaperekeza amenewo pa ulendo wao koyenera Mulungu, udzacita bwino:

7. pakuti cifukwa ca dzinali anaturuka, osalandira kanthu kwa amitundu.

3 Yohane 1