3 Yohane 1:12-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Demetriyo, adamcitira umboni anthu onse, ndi coonadi comwe; ndipo ifenso ticita umboni; ndipo udziwa kuti umboni wathu uli woona.

13. Ndinali nazo zambiriza kukulembera, komatu sindifuna kukulembera ndi kapezi ndi peni;

14. koma ndiyembekeza kukuona iwe msanga, ndipo tidzalankhula popenyana, Mtendere ukhale nawe. Akulankhula abwenzi, Lankhula abwenzi ndi kuchula maina ao.

3 Yohane 1