12. Koma Tukiko ndamtuma ku Efeso.
13. Copfunda cija ndinacisiya ku Trowa kwa Karpo, udze naco pakudza iwe, ndi mabuku, makamaka zikopa zija zolembedwa.
14. Alesandro wosula mkuwa anandicitira zoipa zambiri: adzambwezera iye Ambuye monga mwa nchito zace;
15. ameneyo iwenso ucenjere naye; pakuti anatsutsana nao mau athu.