2 Timoteo 1:12-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Cifukwa ca ideo ndinamva zowawa izi; komatu sindicita manyazi; pakuti ndimdziwa iye amene ndamkhulupirira, ndipo ndikopeka mtima kuti ali wa mphamvu ya kudikira cosungitsa eangaeo kufikira tsiku lijalo.

13. Gwira citsanzo ca mau a moyo, amene udawamva kwa ine, mwa cikhulupiriro ndi cikondi ciri mwa Kristu Yesu.

14. Cosungitsa cokomaca udikire mwa Mzimu Woyera amene akhalitsa mwa ife.

15. Ici ucidziwa, kuti onse a m'Asiya adabwerera kusiyana nane; a iwo ali Fugelo ndi Hermogene,

16. Ambuye acitire banja la Onesiforo cifundo; pakuti anatsitsimutsa ine kawiri kawiri, ndipo sanacita manyazi ndi unyolo wanga;

17. komatu pokhala m'Roma iye anandifunafuna ine ndi khama, nandipeza,

18. (Ambuye ampatse iye apeze cifundo ndi Ambuye tsiku lijalo); ndi muja ananditumikira m'zinthu zambiri m'Efeso, uzindikira iwe bwino.

2 Timoteo 1