2 Samueli 8:15-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo Davide anakhala mfumu ya Aisrayeli onse, Davide naweruza ndi cilungamo mirandu ya anthu onse.

16. Ndipo Yoabu mwana wa Zeruya anayang'anira ankhondo, ndi Josafati mwana wa Ahiludi anali wolemba mbiri,

17. ndi Zadoki mwana wa Ahitubi, ndi Ahimeleki mwana wa Abyatara anali ansembe, ndi Seraya anali mlembi.

18. Ndipo Benaya mwana wa Jehoyada anayang'anira Akereti ndi Apeleti. Ndipo ana a Davide anali nduna zace.

2 Samueli 8