2 Samueli 22:4-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndidzaitanakwa Yehovaamene ayenera timtamande;Comweco ndidzapulumutsidwa kwa adani anga.

5. Pakuti mafunde a imfa anandizinga,Mitsinje ya zopanda pace inandiopsa ine.

6. Zingwe za kumanda zinandizingira;Misampha ya imfa inandifikira ine.

7. M'kusauka kwanga ndinaitana kwa Yehova,Inde ndinakuwira kwa Mulungu wanga;Ndipo Iye anamva mau anga ali m'kacisi wace,Ndi kulira kwanga kunafika ku makutuace.

8. Pomwepo dziko linagwedezeka ndi kunthunthumira.Maziko a dziko la kumwamba anasunthikaNagwedezeka, cifukwa iye anakwiya.

9. M'mphuno mwace munaturuka utsi,Ndi moto woturuka m'kamwa mwace unaononga;Makala anayaka nao.

10. Anaweramitsa miyambanso, natsika;Ndipo mdima wandiwe-yani unali pansi pa mapazi ace.

11. Ndipo iye anaberekeka pa Kerubi nauluka;Inde anaoneka pa mapiko a mphepo,

2 Samueli 22