2 Samueli 22:13-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Ceza ca pamaso paceMakala a mota anayaka,

14. Yehova anagunda kumwamba;Ndipo Wam'mwambamwamba ananena mau ace.

15. Ndipo iye anatumiza mibvi, nawawaza;Mphezi, nawaopsa,

16. Pamenepo m'munsi mwa nyanja munaoneka,Maziko a dziko anaonekera poyera,Ndi mthonzo wa Yehova,Ndi mpumo wa mweya wa m'mphuno mwace.

17. Iye anatumiza kucokera kumwamba nanditenga;Iye ananditurutsa m'madzi akuru;

18. Iye anandipulumutsa kwa mdani wanga wamphamvu,Kwa iwo akudana ndi ine; pakuti anandiposa mphamvu,

19. Anandifikira ine tsiku la tsoka langa;Koma Yehova anali mcirikizo wanga,

20. Iye ananditurutsanso ku malo akuru;Iye anandipulumutsa, cifukwa akondwera ndi ine.

2 Samueli 22