2 Samueli 18:21-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Pamenepo Yoabu ananena ndi Mkusi, Kauze mfumu zimene unaziona. Ndipo Mkusi anawerama kwa Yoabu, nathamanga.

22. Ndipo Ahimaazi mwana wa Zadoki ananena kaciwiri kwa Yoabu, Komatu, mundilole ndithamange inenso kutsata Mkusi. Ndipo Yoabu anati, Udzathamangiranji, mwana wanga, popeza sudzalandira mphotho ya pa mauwo?

23. Koma ngakhale kotero, anati iye, Ndithamange, iye nanena naye, Thamanga. Ndipo Ahimaazi anathamanga njira ya kucigwa, napitirira Mkusi.

24. Koma Davide anakhala pakati pa zipata ziwiri; ndipo mlonda anakwera pa tsindwi la cipata ca kulinga, natukula maso ace, napenya; naona munthu alikuthamanga yekha.

25. Pamenepo mlondayo anapfuula, nauza mfumu. Mfumuyo niti, Ngati ali yekha alikubwera ndi mau. Ndipo iye uja anayenda msanga, nayandikira.

2 Samueli 18