2 Samueli 15:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, citapita ici Abisalomu anadzikonzera gareta ndi akavalo ndi anthu makumi asanu akuthamanga momtsogolera.

2. Ndipo Abisalomu analawirira, nakaima pa njira ya kucipata; ndipo kunatero, pakakhala munthu ali yense ndi mrandu woyenera kufika kwa mfumu kuti aweruze, Abisalomu anamuitana, nati, Ndinu wa ku mudzi uti? Ndipo anati, Mnyamata wanu; ndiye wa pfuko tina la Aisrayeli.

3. Abisalomu nanena naye, Ona zokamba zako ndizo zabwino ndi zolungama; koma mfumu sinauze wina kuti adzamve za iwe.

2 Samueli 15