2 Petro 3:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. ndi kuyamba kucizindikira ici kuti masiku otsiriza adzafika onyoza ndi kucita zonyoza, oyenda monga mwa zilakolako za iwo eni,

4. ndi kunena, Liri kuti lonjezano la kudza kwace? pakuti kuyambira kuja makolo adamwalira zonse zikhala monga ciyambire cilengedwe.

5. Pakuti ici aiwala dala, kuti miyamba inakhala kale lomwe, ndi dziko lidaungika ndi madzi ndi mwa madzi, pa mau a Mulungu;

6. mwa izi dziko lapansi la masiku aja, pomizika ndi madzi, lidaonongeka;

2 Petro 3