2 Mbiri 7:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Atatha tsono Solomo kupemphera, moto unatsika kumwamba, nunyeketsa nsembe yopsereza, ndi nsembe zophera; ndipo ulemerero wa Yehova unadzaza nyumbayi.

2. Ndipo ansembe sanakhoza kulowa m'nyumba ya Yehova, popeza ulemerero wa Yehova unadzaza nyumba ya Yehova.

3. Ndi ana onse a Israyeli anapenyerera potsika motowo, ndi pokhala ulemerero wa Yehova panyumbayi; nawerama nkhope zao pansi poyalidwa miyala, nalambira, nayamika Yehova, nati, Pakuti Iye ndiye wabwino, pakuti cifundo cace cikhala cikhalire.

2 Mbiri 7