10. Ndipo Yehova wakhazikitsa mau ace adanenawo, pakuti ndinauka ine m'malo mwa Davide atate wanga, ndipo ndikhala pa mpando wacifumu wa Israyeli monga analonjeza Yehova, ndipo ndamangira dzina la Yehova Mulungu wa Israyeli nyumbayi.
11. Ndipo ndalongamo likasa, muli cipangano ca Yehova, anacicita ndi ana a Israyeli.
12. Ndipo Solomo anaima ku guwa la nsembe la Yehova pamaso pa khamu lonse la Israyeli, natambasula manja ace.
13. Ndipo Solomo adapanga ciunda camkuwa, m'litali mwace mikono isanu, ndi kupingasa kwace mikono isanu, ndi msinkhu wace mikono itatu, naciika pakati pa bwalo; ndipo anaima pamenepo, nagwada pa maondo ace pamaso pa khamu lonse la Israyeli, natambasulira manja ace kumwamba;