2 Mbiri 5:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Momwemo zidatha nchito zonse Solomo adazicitira nyumba ya Yehova. Ndipo Solomo anabwera nazo zopatulika zija za atate wace Davide; naziika siliva, ndi golidi, ndi zipangizo zonse m'cuma ca nyumba ya Mulungu.Kuperekedwa kwa Kacisi.

2. Pamenepo Solomo anasonkhanitsira akulu akulu a Israyeli, ndi akuru onse a mafuko, ndi akalonga a nyumba za makolo a ana a Israyeli, ku Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova ku mudzi wa Davide ndiwo Zioni.

3. Ndipo amuna onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu kumadyerero anacitikawo, m'mwezi wacisanu ndi ciwiri.

4. Nadza akulu akulu onse a Israyeli, nanyamula likasalo Alevi.

5. Ndipo anakwera nalo likasa, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika zinali m'cihemamo; izizo ansembe Alevi anakwera nazo.

2 Mbiri 5