20. Ndi Yerobiamu sanaonanso mphamvu m'masiku a Abiya, namkantha Yehova, wa iye.
21. Koma Abiya anakula mphamvu, nadzitengera akazi khumi ndi anai, nabala ana amuna makumi awiri mphambu awiri, ndi ana akazi khumi mphambu asanu ndi mmodzi.
22. Macitidwe ena tsono a Abiya, ndi mayendedwe ace, ndi mau ace, alembedwa m'buku lomasulira la mneneri Ido.