2 Mbiri 12:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Nadzilimbitsa Rehabiamu mfumu m'Yerusalemu, nacita ufumu; pakuti Rehabiamu anali wa zaka makumi anai mphambu cimodzi polowa ufumu wace, nakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi ziwiri m'Yerusalemu, ndiwo mudzi Yehova adausankha m'mafuko onse a Israyeli, kuikapo dzina lace; ndipo dzina la mace ndiye Naama M-amoni.

14. Koma anacita coipa, popeza sanalunjikitsa mtima wace kufuna Yehova.

15. Macitidwe ace tsono a Rehabiamu, zoyamba ndi zotsiriza, sizilembedwa kodi m'buku la mau a Semaya mneneriyo, ndi la Ido mlauliyo, lakunena za zibadwidwe? Ndipo panali nkhondo pakati pa Rehabiamu ndi Yerobiamu masiku onse.

16. Nagona Rehabiamu ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide; ndipo Abiya mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

2 Mbiri 12