2 Mafumu 9:21-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Nati Yoramu, Manga. Namanga gareta wace, Ndipo Yoramu mfumu ya Israyeli ndi Ahaziya mfumu ya Yuda anaturuka yense m'gareta wace, naturuka kukakomana ndi Yehu, nakomana naye pa munda wa Naboti m'Yezreeli.

22. Ndipo kunali, pamene Yoramu anaona Yehu, anari, Mtendere kodi, Yehu? Nati iye, Ngwanji mtendere pokhala cacuruka cigololo ndi nyanga zace za mai wako Yezebeli?

23. Natembenuza Yoramu manja ace, nathawa, nati kwa Ahaziya, Ciwembu, Ahaziya.

24. Nafa nao Yehu uta wace, nalasa Yoramu pacikota, nuturuka mubvi pa mtima wace, naonyezeka iye m'gareta wace.

2 Mafumu 9