2 Mafumu 6:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo ana a aneneri anati kwa Elisa, Taonani tsono, pamalo tikhalapo ife pamaso panu paticepera

2. Mutilole tipite ku Yordano, tikatengeko, ali yense mtengo, tidzimangire malo komweko, tikhalepo, Nati, Mukani.

3. Ndipo wina anati, Mulole mupite nafe anyamata anu. Nati, Ndidzamuka.

4. Namuka nao, nafika ku Yordano, iwo natema mitengo.

5. Ndipo wina analinkudula mtengo nkhwangwa inagwa m'madzi; ndipo anapfuula, nati, Kalanga ine mbuyanga! popeza ojobwereka.

2 Mafumu 6