2 Mafumu 5:2-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

2. Ndipo Aaramu adaturuka magulu magulu, nabwera nalo m'ndende buthu locokera ku dziko la Israyeli, natumikira mkazi wa Namani iyeyu,

3. Nati uyu kwa mbuyace wamkazi, Mbuye wanga akadakhala kwa mneneri ali m'Samariya, akadamciritsa khate lace.

4. Ndipo analowa wina, nauza mbuye wace, kuti, Buthulo lofuma ku dziko la Israyeli lanena zakuti zakuti.

5. Pamenepo mfumu ya Aramu inati, Tiye, muka, ndidzatumiza kalata kwa mfumu ya Israyeli. Pamenepo anacoka, atatenga siliva: matalente khumi, ndi golidi masekeli zikwi zisanu ndi cimodzi, ndi zobvala zakusintha khumi.

2 Mafumu 5