2 Mafumu 25:18-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

18. Ndipo mkuru wa olindirira anatenga Seraya wansembe wamkulu, ndi Zefaniya wansembe waciwiri, ndi olindira pakhomo atatu;

19. natenga m'mudzimo mdindo woikidwa woyang'anira ankhondo; ndi anthu asanu a iwo openya nkhope ya mfumu opezeka m'mudzimo; ndi mlembi, kazembe wa nkhondo wolembera anthu a m'dziko; ndi anthu a m'dziko makumi asanu ndi limodzi opezeka m'mudzimo.

20. Ndipo Nebuzaradani mkuru wa olindirira anawatenga, napita nao kwa mfumu ya Babulo ku Ribila.

2 Mafumu 25