2 Mafumu 12:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndarama za nsembe zoparamula ndi ndarama za nsembe yaucimo sanabwera nazo ku nyumba ya Yehova; nza ansembe izi.

17. Pamenepo Hazaeli mfumu ya Aramu anakwera, nathira nkhondo pa Gati, naulanda, nalunjikitsa nkhope yace kukwera ku Yerusalemu.

18. Koma Yoasi mfumu ya Yuda: anatenga zopatulika zonse adazipatula Yehosafati, ndi Yoramu, ndi Ahaziya, makolo ace, mafumu a Yuda, ndi zopatulika zace zace, ndi golidi yense anampeza pa cuma ca nyumba ya Yehova, ndi ca nyumba ya mfumu, nazitumiza kwa Hazaeli mfumu ya Aramu; motero anabwerera kucoka ku Yerusalemu.

19. Macitidwe ena tsono a Yoasi ndi zonse adazicita sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

20. Ndipo anyamata ace ananyamuka, napangana, nakantha Yoasi ku nyumba ya Milo potsikira ku Silo.

2 Mafumu 12