2 Atesalonika 3:4-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. koma tikhulupirira mwa Ambuye za inu, kuti mumacita, ndiponso mudzacita zimene tikulamulirani.

5. Ndipo Ambuye atsogolere bwino mitima yanu ilowe m'cikondi ca mulungu ndi m'cipiriro ca Kristu,

6. Ndipo tikulamulirani, abale, m'dzina la Ambuye wathu Yesu Kristu, kuti mubwebvuke kwa mbale yense wakuyenda dwacedwace, wosatsata mwambo umene anaulandira kwa ife.

7. Pakuti mudziwa nokha m'mene muyenera kutitsanza ifemo; pakuti sitinakhala dwacedwace mwa inu;

2 Atesalonika 3