2 Akorinto 8:10-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo m'menemo odichula coyesa ine; pakuti cimene cipindulira inu, amene munayamba kale caka capitaci si kucita kokha, komanso kufunira.

11. Koma tsopano tsirizani kucitaku; kuti monga kunali cibvomerezo ca kufunira, koteronso kukhale kutsiriza kwacem'cimene muli naco.

12. Pakuti ngati cibvomerezoco ciri pomwepo, munthu alandiridwa monga momwe ali naco, si monga cimsowa.

13. Pakuti sinditero kuti ena akamasuke, ndi inu musautsidwe;

14. koma mwa kulingana kucuruka kwanu kukwanire kusowa kwao nthawi ya makono ano, kutinso kucuruka kwao kukwanire kusowa kwanu,

15. Kuti pakhalecilingano; monga kwalembedwa, Wosonkhetsacambiri sicinamtsalira; ndi iye wosonkhetsa pang'ono sicinamsowa.

16. Koma ayamikike Mulungu, wakupatsa khama lomweli la kwa inu mu mtima wa Tito.

17. Pakutitu analandira kudandaulira kwathu; koma pokhala halo khama loposa, anaturukira kunka kwil inu mwini wace.

18. Ndipo tatuma pamodzi naye mbaleyo, amene kusimba kwace m'Uthenga Wabwino kuli m'Mipingo yonse;

19. ndipo si ici cokha, komanso anasankhika ndi Mipingo, apite limodzi ndi ife m'cisomo ici, cimene ticitumikira ife, kwa ulemerero wa Ambuye, ndi kuonetsa cibvomerezo cathu;

20. ndi kupewa ici kuti wina angatichule za kucurukira kumene tikutumikira;

21. pakuti tikonzeratu zinthu zokoma, si pamaso pa Ambuye pokha, komanso pamaso pa anthu.

2 Akorinto 8