2 Akorinto 6:5-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. m'mikwingwirima, m'ndende, m'mapokoso, m'mabvutitso, m'madikiro, m'masalo a cakudya;

6. m'mayeredwe, m'cidziwitso, m'cilekerero, m'kukoma mtima, mwa Mzimu Woyera, m'cikondi cosanyenga;

7. m'mau a coonadi, mu mphamvu ya Mulungu; mwa camuna ca cilungamo kulamanja ndi kulamanzere,

8. mwa ulemerero, mwa mnyozo, mwa mbiri yoipa ndi mbiri yabwino; mongaosoceretsa, angakhale ali oona;

9. monga osadziwika, angakhale adziwika bwino; monga alinkufa, ndipo taonani, tiri ndi moyo; monga olangika, ndipo osaphedwa;

10. monga akumva cisoni, koma akukondwera nthawi zonse; monga aumphawi, lroma akulemeretsa ambiri; mensa okhala opanda-kanthu, ndipo akhala nazo zinthu zonse.

11. M'kamwa mwathu mmotseguka kwa inu Akorinto, mtima wathu wakulitsidwa.

12. Simupsinjika mwa ife, koma mupsiniika mumtima mwanu.

2 Akorinto 6