7. (pakuti tiyendayenda mwa cikhulupiriro si mwa cionekedwe);
8. koma tilimbika mtima, ndipo tikondwera makamaka kusakhala m'thupi, ndi kukhala kwathu kwa Ambuye.
9. Cifukwa cacenso tifunitsitsa, kapena kwathu kapena kwina, kukhala akumkondweretsa iye.
10. Pakuti ife tonse tiyenera kuonetsedwa ku mpando wa kuweruza wa Kristu, kuti yense alandire zocitika m'thupi, monga momwe anacita, kapena cabwino kapena coipa.