5. Ndipo wotikonzera ife ici cimene, ndiye Mulungu, amene anatipatsa ife cikhole ca Mzimu,
6. Pokhala nako kulimbika mtima nthawi zonse tsono, ndipo podziwa kuti pamene tiri kwathu m'thupi, sitiri kwa Ambuye,
7. (pakuti tiyendayenda mwa cikhulupiriro si mwa cionekedwe);
8. koma tilimbika mtima, ndipo tikondwera makamaka kusakhala m'thupi, ndi kukhala kwathu kwa Ambuye.
9. Cifukwa cacenso tifunitsitsa, kapena kwathu kapena kwina, kukhala akumkondweretsa iye.