2 Akorinto 11:25-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Katatu ndinamenyedwa ndi ndodo, kamodzi ndinaponyedwa miyala, katatu ndinatayika posweka combo, ndinakhala m'kuya tsiku limodzi usana ndi usiku;

26. paulendo kawiri kawiri, moopsya mwace mwa mitsinje, moopsya mwace mwa olanda, 1 moopsya modzera kwa mtundu wanga, moopsya modzera kwa amitundu, moopsya m'mudzi, moopsya m'cipululu, moopsya m'nyanja, moopsya mwaabale onyenga;

27. m'cibvutitso ndi m'colemetsa, m'madikiro kawiri kawiri, 2 m'njala ndi ludzu, m'masalo a cakudyakawiri kawiri, m'cisanu ndi umarisece.

28. Popanda zakunjazo pali condisindikiza tsiku ndi tsiku, calabadiro ca Mipingo yonse.

29. 3 Afoka ndani wosafoka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

30. Ngati ndiyenerakudzitamandira, 4 ndidzadzitamandira ndi za kufoka kwanga.

31. Mulungu Atate wa Ambuye Yesu, iye amene alemekezeka ku nthawi yonse, adziwa kuti sindinama.

2 Akorinto 11