1. Tiana tanga, izi ndikulemberani, kuti musacimwe. Ndipo akacimwa wina, Nkhoswe tiri naye kwa Atate, ndiye Yesu Kristu wolungama;
2. ndipo iye ndiye ciombolo ca macimo athu; koma wosati athu okha, komanso a dziko lonse lapansi.
3. Ndipo umo tizindikira kuti tamzindikira iye, ngati tisunga malamulo ace.