1 Samueli 25:39-41 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo pamene Davide anamva kuti Nabala adamwalira, iye anati, Alemekezedwe Yehova, amene anaweruza mrandu wa mtonzo wanga wocokera ku dzanja la Nabala, naletsa mnyamata wace pa coipa; ndipo Yehova anabwezera pamutu pa Nabala coipa cace. Ndipo Davide anatumiza wokamfunsira Abigayeli, zakuti amtengere akhale mkazi wace.

40. Ndipo anyamata a Davide pakufika kwa Abigayeli ku Karimeli, analankhula naye, nati, Davide anatitumiza kwa inu, kukutengani, mukhale mkazi wace.

41. Ndipo iye ananyamuka, nawerama nkhope yace pansi, nati, Onani, mdzakazi wanu ali kapolo wakusambitsa mapazi a anyamata a mbuye wanga.

1 Samueli 25