1 Samueli 2:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Musalankhulenso modzikuza kwambiri motero;M'kamwa mwanu musaturuke zolulutsa;Cifukwa Yehova ali Mulungu wanzeru,Ndipo iye ayesa zocita anthu.

4. Mauta a amphamvu anathyoka,Koma okhumudwawo amangiridwa ndi mphamvu m'cuuno.

5. Amene anakhuta anakasuma cakudya;Koma anjalawo anacira;Inde cumba cabala asanu ndi awiri:Ndipo iye amene ali ndi ana ambiri acita liwondewonde.

6. Yehova amapha, napatsa moyo:Iye amatsitsa kumanda, naukitsanso.

7. Yehova asaukitsa, nalemeza;Acepetsa, nakuzanso.

1 Samueli 2