1 Petro 4:9-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. mucerezane wina ndi mnzace, osadandaula:

10. monga yense walandira mphatso, mutumikirane nayo, ngati adindo okoma a cisomo ca mitundu mitundu ca Mulungu;

11. akalankhula wina, alankhule ngati manenedwe a Mulungu; wina akatumikira, acite ngati mu mphamvu imene Mulungu ampatsa, kuti m'zonse Mulungu alemekezedwe mwa Yesu Kristu, amene ali nao ulemerero ndi mphamvu ku nthawi za nthawi. Amen.

12. Okondedwa, musazizwe ndi mayesedwe amoto adakugwerani inu akhale cakukuyesani, ngati cinthu cacilendo cacitika nanu:

13. koma popeza mulawana ndi Kristu zowawa zace, kondwerani; kutinso pa bvumbulutso la ulemerero wace mukakondwere kwakukurukuru.

1 Petro 4