1 Petro 1:13-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Mwa ici, podzimanga m'cuuno, kunena za mtima wanu, mukhale odzisunga, nimuyembekeze konse konse cisomo cirikutengedwa kudza naco kwa inu m'bvumbulutso la Yesu Kristu;

14. monga ana omvera osadzifanizitsanso ndi zilakolako zakale, pokhala osadziwa inu;

15. komatu monga iye wakuitana inu ali woyera mtima, khaiani inunso oyera mtima m'makhalidwe anu onse;

16. popeza kwalembedwa, Muzikhala oyera mtima, pakuti Ine ndine woyera mtima.

17. Ndipo mukamuitana ngati Alate, iye amene aweruza monga mwa nchito ya yense, wopanda tsankhu, khalani ndi mantha nthawi ya cilendo canu;

1 Petro 1