17. Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.
18. Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.
19. Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.
20. Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.
21. Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.
22. Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.
23. A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;