1 Mbiri 26:17-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.

18. Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.

19. Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.

20. Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.

21. Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.

22. Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.

23. A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;

1 Mbiri 26