16. Supimu ndi Hosa kumadzulo, ku cipata ca Saleketi, ku mseu wokwerapo, udikiro pandunji pa udikiro.
17. Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.
18. Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.
19. Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.