6. Ndi Semaya mwana wa Netaneli mlembi, ndiye wa Alevi, anawalembera pamaso pa mfumu; ndi akalonga, ndi Zadoki wansembe, ndi Ahimeleke mwana wa Abyatara, a akuru a nyumba za makolo a ansembe ndi Alevi, anatenga nyumba imodzi ya kholo lace ya Eleazara, ndi imodzi ya Itamara.
7. Ndipo maere oyamba anamgwera Yehoyaribu, waciwiri Yedaya,
8. wacitatu Harimu, wacinai Seorimu,
9. wacisanu Malikiya, wacisanu ndi cimodzi Miyamini,
10. wacisanu ndi ciwiri Hakozi, wacisanu ndi citatu Abiya,
11. wacisanu ndi cinai Yesuwa, wakhumi Sekaniya,
12. wakhumi ndi cimodzi Eliyasibu, wakhumi ndi ciwiri Yakimu,
13. wakhumi ndi citatu Hupa, wakhumi ndi cinai Yesebeabu,
14. wakhumi ndi cisanu Biliga, wakhumi ndi cisanu ndi cimodzi Imeri,
15. wakhumi ndi cisanu ndi ciwiri Heziri, wakhumi ndi cisanu ndi citatu Hapizezi,
16. wakhumi ndi cisanu ndi cinai Petahiya, wa makumi awiri Yehezikeli,
17. wa makumi awiri ndi cimodzi Yakini, wa makumi awiri ndi ciwiri Gamuli,
18. wa makumi awiri ndi citatu Delaya, wa makumi awiri ndi cinai Miziya.
19. Awa ndi malongosoledwe ao m'utumiki wao kulowa m'nyumba ya Yehova, monga mwa ciweruzo adawapatsa Aroni atate wao, monga Yehova Mulungu wa Israyeli anamlamulira.
20. Ndipo wa ana otsala a Levi: wa ana a Amiramu, Subaeli; wa ana a Subaeli, Yedeya.
21. Wa Rehabiya: wa ana a Rehabiya, mkuru ndi Isiya.
22. Wa Aizari: Selomoti; wa ana a Selomoti, Yahati.
23. Ndi wa ana a Hebroni: mkuru ndi Yeriya, waciwiri Amariya, wacitatu Yahazieli, wacinai Yekameamu.