15. Ana a Mose: Gerisomu, ndi Eliezeri.
16. Ana a Gerisomu: wamkuru ndi Sebuyeli.
17. Ndi ana a Eliezeri: wamkuru ndi Rehabiya. Ndipo Eliezeri analibe ana ena, koma ana a Rehabiya anacuruka kwambiri.
18. Ana a Izara: wamkuru ndiye Selomiti.
19. Ana a Hebroni: wamkuru ndi Yeriya, waciwiri ndi Amariya, wacitatu ndi Yehazieli, wacinai ndi Yekameamu,
20. Ana a Uzieli: wamkuru ndi Mika, waciwiri ndi Isiya.
21. Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi ana a Mali: Eleazara ndi Kisi.
22. Nafa Eleazara wopanda ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndi asuweni ao ana a Kisi anawatenga akhale akazi ao.
23. Ana a Musi: Mali, ndi Ederi, ndi Yeremoti; atatu.