1 Mbiri 23:14-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Kunena za Mose munthu wa Mulunguyo, ana ace anaehulidwa mwa pfuko la Levi.

15. Ana a Mose: Gerisomu, ndi Eliezeri.

16. Ana a Gerisomu: wamkuru ndi Sebuyeli.

17. Ndi ana a Eliezeri: wamkuru ndi Rehabiya. Ndipo Eliezeri analibe ana ena, koma ana a Rehabiya anacuruka kwambiri.

18. Ana a Izara: wamkuru ndiye Selomiti.

19. Ana a Hebroni: wamkuru ndi Yeriya, waciwiri ndi Amariya, wacitatu ndi Yehazieli, wacinai ndi Yekameamu,

20. Ana a Uzieli: wamkuru ndi Mika, waciwiri ndi Isiya.

21. Ana a Merari: Mali ndi Musi. Ndi ana a Mali: Eleazara ndi Kisi.

22. Nafa Eleazara wopanda ana amuna, koma ana akazi ndiwo; ndi asuweni ao ana a Kisi anawatenga akhale akazi ao.

23. Ana a Musi: Mali, ndi Ederi, ndi Yeremoti; atatu.

1 Mbiri 23