1 Mbiri 22:17-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

17. Davide analangizanso akalonga a Israyeli athanelize Solomo mwana wace, ndi kuti,

18. Kodi Yehova Mulungu wanu sali nanu? sanakupumulitsani pambali ponse? pakuti anapereka nzika za m'dziko m'dzanja mwanga, ndi dziko lagonjetsedwa pamaso pa Yehova, ndi pamaso pa anthu ace.

19. Perekani tsono mtima ndi moyo wanu kufunafuna Yehova Mulungu wanu; ndipo nyamukani ndi kumanga malo opatulika a Yehova Mulungu, kuti abwere nalo likasa la cipangano la Yehova, ndi zipangizo zopatulika za Mulungu, ku nyumba imene idzamangidwira dzina la Yehova.

1 Mbiri 22