1 Mbiri 2:5-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Ana a Perezi: Hezironi, ndi Hamuli.

6. Ndi ana a Zera: Zimri, ndi Etani, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Dara; onse pamodzi ndi asanu.

7. Ndi ana a Karmi: Akari wobvuta Israyeliyo, amene analakwira coperekedwa ciperekereco.

8. Ndi mwana wa Etani: Azariya.

9. Ndi ana a Hezironi anambadwirawo: Yerameli, ndi Ramu, ndi Kelubai.

10. Ndi Ramu anabala Aminadabu; ndi Aminadabu anabala Nasoni kalonga wa ana a Yuda;

11. ndi Nasoni anabala Salima, ndi Salima anabala Boazi,

12. ndi Boazi anabala Obedi, ndi Obedi anabala Jese,

13. ndi Jese anabala mwana wace wamwamuna woyamba Eliabu, ndi Abinadabu waciwiri, ndi Simeya wacitatu,

14. Netaneli wacinai, Radai wacisanu,

15. Ozemu wacisanu ndi cimodzi, Davide wacisanu ndi ciwiri;

16. ndi alongo ao ndiwo Zeruya ndi Abigaili. Ndi ana a Zeruya: Abisai ndi Yoabu, ndi Asaheli; atatu.

17. Ndi Abigaili anabala Amasa; ndi atate wa Amasa ndiye Yeteri M-ismayeli.

1 Mbiri 2