1 Mbiri 2:4-12 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndi Tamari mpongozi wace anambalira Perezi ndi Zera. Ana amuna onse a Yuda ndiwo asanu.

5. Ana a Perezi: Hezironi, ndi Hamuli.

6. Ndi ana a Zera: Zimri, ndi Etani, ndi Hemani, ndi Kalikoli, ndi Dara; onse pamodzi ndi asanu.

7. Ndi ana a Karmi: Akari wobvuta Israyeliyo, amene analakwira coperekedwa ciperekereco.

8. Ndi mwana wa Etani: Azariya.

9. Ndi ana a Hezironi anambadwirawo: Yerameli, ndi Ramu, ndi Kelubai.

10. Ndi Ramu anabala Aminadabu; ndi Aminadabu anabala Nasoni kalonga wa ana a Yuda;

11. ndi Nasoni anabala Salima, ndi Salima anabala Boazi,

12. ndi Boazi anabala Obedi, ndi Obedi anabala Jese,

1 Mbiri 2