1 Mbiri 15:4-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Ndipo Davide anasonkhanitsa ana a Aroni ndi Alevi;

5. a ana a Kohati, Urieli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi awiri;

6. a ana a Merari, Adaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri mphambu makumi awiri;

7. a ana a Gerisomu, Yoeli mkuru wao, ndi abale ace zana limodzi mphambu makumi atatu;

8. a ana a Elizafana, Semaya mkuru wao, ndi abale ace mazana awiri;

9. a ana a Hebroni, Elieli mkuru wao, ndi abale ace makumi asanu ndi atatu;

1 Mbiri 15