21. ndi Matitiya, ndi Elifelehu, ndi Mikeya, ndi Obedi Edomu, ndi Yeieli, ndi Azaziya, ndi azeze akuyimbira mwa Seminiti, kutsogolera mayimbidwe.
22. Ndi Kenaniya mkuru wa Alevi anayang'anira kusenzako; anawalangiza za kusenza, pakuti anali waluso.
23. Ndi Berekiya ndi Elikana anali odikira likasa.