1 Mbiri 15:16-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ndipo Davide ananena ndi mkuru wa Alevi kuti aike abale ao oyimbawo ndi zoyimbira, zisakasa, ndi azeze, ndi nsanje, azimveketse ndi kukweza mau ao ndi cimwemwe.

17. Ndipo Alevi anaika Hemani mwana wa Yoeli, ndi a abale ace Asafu mwana wa Berekiya, ndi a ana a Merari, abale ao, Etani mwana wa Kusaya;

18. ndi pamodzi nao abale ao a kulongosola kwaciwiri, Zekariya, Beni, ndi Yaazieli, ndi Semiramoti, ndi Yehieli, ndi Uni, Bliabu, ndi Benaya, ndi Maaseya, ndi Matitiya, ndi Blifelehu, ndi Mikineya, ndi Obedi Bdomu, ndi Yeieli, ndikirawo.

19. Oyimba tsono: Hemani, Asafu, ndi Btani, anayimba ndi nsanje zamkuwa;

20. ndi Zekariya, ndi Azieli, ndi Semiramod, ndi Yehieli, ndi Uni, ndi Bliabu, ndi Maaseya, ndi Benaya, ndi zisakasa kuyimbira mwa Alimoti;

1 Mbiri 15