1 Mafumu 7:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndi pamwamba pace panali miyala ya mtengo wapatali, ndiyo miyala yosemasema monga muyeso wace, ndi mitengo yamkungudza.

12. Ndipo bwalo lalikuru lozingapo linali ndi mizere itatu ya miyala yosemasema, ndi mzere umodzi wa mitanda yamkungundza, monga bwalo la pakati pa nyumba ya Yehova, ndi likole la nyumbayo.

13. Ndipo mfumu Solomo anatuma anthu kukatenga Hiramu ku Turo.

14. Iyeyo anali mwana wace wa mkazi wamasiye wa pfuko la Nafitali, atate wace anali munthu wa ku Turo, mfundi wa mkuwa; ndipo iye anadzala ndi nzeru ndi luntha ndi luso kugwira nchito zonse za mkuwa. Ndipo anadza kwa mfumu Solomo namgwirira nchito zace zonse.

1 Mafumu 7