1 Mafumu 11:39-43 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo cifukwa ca ici nelidzazunza mbumba ya Davide, koma si masiku onse ai.

40. Cifukwa cace Solomo anafuna kupha Yerobiamu, ndipo Yerobiamu anathawira ku Aigupto kwa Sisaki mfumu ya Aigupto, nakhala m'Aigupto kufikira imfa ya Solomo.

41. Ndipo macitidwe otsiriza a Solomo, ndi nchito zace zonse anazicita, ndi nzeru zace, kodi sizilembedwa zimenezo m'buku la madtidwe a Solomo?

42. Ndipo masiku amene Solomo anakhala mfumu ya Aisrayeli onse m'Yerusalemu anali zaka makumi anai.

43. Ndipo Solomo anagona ndi makolo ace, naikidwa m'mudzi wa Davide atate wace; ndipo Rehabiamu mwana wace anakhala mfumu m'malo mwace.

1 Mafumu 11