2. Pakuti inu nokha mudziwa bwino kuti tsiku la Ambuye lidzadza monga mbala usiku,
3. Pamene angonena, Mtendere ndi mosatekeseka, pamenepo cionongeko cobukapo cidzawagwera, monga zowawa mkazi wa pakati; ndipo sadzapulumuka konse.
4. Kama inu, abale, simuli mumdima, kuti tsikulo likakugwereni monga mbala;
5. pakuti inu nonse muli ana a kuunika, ndi ana a usana; sitiri a usiku, kapena a mdima;
6. cifukwa cace tsono tisagone monga otsalawo, komatu tidikire, ndipo tisaledzere,
7. Pakuti iwo akugona agona usiku; ndi iwo akuledzera aledzera usiku.