15. Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.
16. Kondwerani nthawi zonse;
17. Pempherani kosaleka;
18. M'zonse yamikani; pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu ca kwa inu, mwa Kristu Yesu.
19. Musazime Mzimuyo;
20. Musanyoze maaenero;
21. Yesani zonse; sungani cokomaco,
22. Mupewe maonekedwe onse a coipa.