1 Atesalonika 5:13-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. ndipo muwacitire ulemu woposatu mwa cikondi, cifukwa ca nchito yao. Khalani mumtendere mwa inu nokha.

14. Koma tidandaulira inu abale, yambirirani ampwayi, limbikitsani amantha mtima? cirikizani ofok a, mukhale oleza mtima pa onse.

15. Penyani kuti wina asabwezere coipa womcitira coipa; komatu nthawi zonse mutsatire cokoma, kwa anzanu, ndi kwa onse.

16. Kondwerani nthawi zonse;

17. Pempherani kosaleka;

18. M'zonse yamikani; pakuti ici ndi cifuniro ca Mulungu ca kwa inu, mwa Kristu Yesu.

19. Musazime Mzimuyo;

20. Musanyoze maaenero;

21. Yesani zonse; sungani cokomaco,

22. Mupewe maonekedwe onse a coipa.

23. Ndipo Mulungu wa mtendere yekha ayeretse inu konsekonse; ndipo mzimu wanu ndi moyo wanu ndi thupi lanu zisungidwe zamphumphu, zopanda cirema pa kudza kwace kwa: Ambuye wathu Yesu Kristu.

1 Atesalonika 5