4. Ndipo ngati kuyenera kwa ine kupitanso, adzapita nane.
5. Koma ndidzadza kwa inu, nditapyola Makedoniya; pakuti ndidzapyola Makedoniya;
6. ndipo kapena ndidzakhalitsa ndi inu, kapenanso kugonera nyengo yacisanu kuti mukandiperekeze ine kumene kuli konse ndipitako,
7. Pakuti sindifuna kukuonani tsopano popitirira; pakuti ndiyembekeza kukhala ndi inu nthawi, ngati alola Ambuye.