1 Akorinto 14:11-15 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Cifukwa cace, ngati sindidziwa mphamvu ya mauwo ndidzakhala kwa iye wolankhulayo wakunja, ndipo wolankhulayo adzakhala wakunja kwaine.

12. Momwemo inunso, popeza muli ofunits its a mphatso zauzimu, funani kuti mukacuruke kukumangirira kwa Mpingo,

13. Cifukwa cace wolankhula lilime, apemphere kuti amasule.

14. Pakuti ngati ndipemphera m'lilime, mzimu wanga upemphera, koma cidziwitso canga cikhala cosabala kanthu.

15. Kuli ciani tsono? Ndidzapemphera ndi mzimu, koma ndidzapempheranso ndi cidziwitso canga; ndidzayimba ndi mzimu, koma ndidzayimbanso ndi cidziwitso.

1 Akorinto 14